Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 4:26-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Yesu ananena naye, Ine wakulankhula nawe ndine amene.

27. Ndipo pamenepo anadza ophunzira ace; nazizwa kuti analinkulankhula ndi mkazi; koma panalibe wina anati, Mufuna ciani? kapena, mulankhula naye ciani?

28. Pamenepo mkazi anasiya mtsuko wace, namuka kumudzi, nanena ndi anthu,

29. Tiyeni, mukaone munthu, amene anandiuza zinthu ziri zonse ndinazicita: ameneyu sali Kristu nanga?

30. Anaturuka iwo m'mudzi ndipo analinkudza kwa iye.

31. Pa mphindikati iyi ophunzira ace anampempha iye, ndi kunena, Rabi, idyani.

32. Koma iye anati kwa iwo, Ine ndiri naco cakudya cimene inu simucidziwa.

33. Cifukwa cace ophunzira ananena wina ndi mnzace, Kodi pali wina anamtengera iye kanthu kakudya?

34. Yesu ananena nao, Cakudya canga ndico kuti ndicite cifuniro ca iye amene anandituma Ine, ndi kutsiriza nchito yace.

35. Kodi simunena inu, kuti, Yatsala miyezi inai, ndipo kudza kumweta? Onani ndinena kwa inu, Kwezani maso anu, nimuyang'ane m'minda, kuti mwayera kale kufikira kumweta.

36. Wakumweta alandira kulipira, nasonkhanitsira cobala ku moyo wosatha; kuti wofesayo akakondwere pamodzi ndi womwetayo.

Werengani mutu wathunthu Yohane 4