Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 4:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Yesu ananena kwa iye, Muka, kamuitane mwamuna wako, nudze kuno.

17. Mkazi anayankha nati kwa iye, Ndiribe mwamuna. Yesu ananena naye, Wanena bwino, kuti mwamuna ndiribe;

18. pakuti wakhala nao amuna asanu; ndipo iye amene ukhala nave tsopano sali mwamuna wako; ici wanena zoona.

19. Mkazi ananena ndi iye, Ambuye, ndizindikira kuti muli Mneneri.

20. Makolo athu analambira m'phiri ili; ndipo inu munena, kuti m'Yerusalemu muli malo ozenera kulambiramo anthu.

21. Yesu ananena naye, Tamvera Ine, mkazi iwe, kuti ikudza nthawi, imene simudzalambira Atate kapena m'phiri ili, kapena m'Yerusalemu.

Werengani mutu wathunthu Yohane 4