Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 4:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. koma iye wakumwa madzi amene Ine ndidzampatsa sadzamva ludzu nthawi zonse; koma madzi amene Ine ndidzampatsa adzakhala mwa iye kasupe wa madzi otumphukira ku moyo wosatha.

15. Mkaziyo ananena kwa iye, Ambuye, ndipatseni madzi amene, kuti ndisamve ludzu, kapena ndisadze kuno kudzatunga.

16. Yesu ananena kwa iye, Muka, kamuitane mwamuna wako, nudze kuno.

17. Mkazi anayankha nati kwa iye, Ndiribe mwamuna. Yesu ananena naye, Wanena bwino, kuti mwamuna ndiribe;

18. pakuti wakhala nao amuna asanu; ndipo iye amene ukhala nave tsopano sali mwamuna wako; ici wanena zoona.

19. Mkazi ananena ndi iye, Ambuye, ndizindikira kuti muli Mneneri.

20. Makolo athu analambira m'phiri ili; ndipo inu munena, kuti m'Yerusalemu muli malo ozenera kulambiramo anthu.

Werengani mutu wathunthu Yohane 4