Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 2:10-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. nanena naye, Munthu ali yense amayamba kuika vinyo wokoma; ndipo anthu atamwatu, pamenepo wina wosakoma; koma iwe wasunga vinyo wokoma kufikira tsopano lino.

11. Ciyambi ici ca zizindikilo zace Yesu anacita m'Kana wa m'Galileya naonetsera ulemerero wace; ndipo akuphunzira ace anakhulupirira iye.

12. Zitapita izianatsikira ku Kapemao, iye ndi amace, ndiabale ace, ndi ophunzira ace; nakhala komweko masiku owerengeka.

13. Ndipo Paskha wa Ayuda unayandikira, ndipo Yesu anakwera kunka ku Yerusalemu.

14. Ndipo anapeza m'Kacisiiwo akugulitsa ng'ombe ndi nkhosa ndi nkhunda, ndi akusinthana ndalama alikukhala pansi.

15. Ndipo pamene adapanga mkwapulo wazingwe, anaturutsa onse m'Kacisimo, ndi nkhosa ndi ng'ombe; nakhuthula ndalama za osinthanawo, nagubuduza magome;

16. nati kwa iwo akugulitsa nkhunda, Cotsani izi muno; musamayesa nyumba ya Atate wanga nyumba ya malonda.

17. Akuphunzira ace anakumbukila kuti kunalembedwa, Cangu ca pa nyumba yanu candidya ine.

18. Cifukwa cace Ayuda anayankha nati kwa iye, Mutionetsera ife cizindikilo canji, pakuti mucita izi?

19. Yesu anayankha nati kwa iwo, Pasulani kacisi uyu, ndipo masiku atatu ndidzamuutsa.

20. Pamenepo Ayuda anati, Zaka makumi anai ndi zisanu ndi cimodzi analimkumanga Kacisiyu, kodi inu mudzamuutsa masiku atatu?

21. Koma iye analikunena za kacisi wathupi lace.

22. Cifukwa cace atauka kwa akufa, akuphunzira ace anakumbukira kuti ananena ici; ndipo anakhulupirira colemba, ndi mau amene Yesu ananena.

23. Koma pamene anali m'Yerusalemu pa Paskha paphwando, ambiri anakhulupirira dzinalace, pakuona zizindikilo zace zimene anaeitazi.

24. Koma Yesu sanakhulupirira iwo kuti akhale nao, cifukwa iye anadziwa anthu onse,

Werengani mutu wathunthu Yohane 2