Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 2:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo tsiku lacitatu pariali ukwati m'Kana wa m'Galileya; ndipo amace wa Yesu anali komweko.

2. Ndipo Yesu yemwe ndi akuphunzira ace anaitanidwa ku ukwatiwo.

3. Ndipo pakutha vinyo, amace wa Yesu ananena naye, Alibe vinyo,

4. Yesu nanena naye, Mkazi, ndiri ndi ciani ndi inu? nthawi yanga siinafike.

5. Amace ananena kwa atumiki, Cimene ciri conse akanena kwa inu, citani.

6. Ndipopanali pamenepo mitsuko yamiyala isanu ndi umodzi yoikidwako monga mwa mayeretsedwe a Ayuda, yonse ya miyeso iwiri kapena itatu.

7. Yesu ananena nao, Dzazani mitsukoyo ndi madzi. Naidzaza, nde nde nde.

Werengani mutu wathunthu Yohane 2