Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 18:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Pamenepo Yudase, m'mene adatenga gulu la asilikari ndi anyamata, kwa ansembe akulu ndi Afarisi, anadza komweko ndi nyali ndi miuni ndi zida.

4. Pamenepo Yesu, podziwa zonse zirinkudza pa iye, anaturuka, nati kwa iwo, Mufuna yani?

5. Anayankha iye, Yesu Mnazarayo. Yesu ananena nao, Ndine. Koma Yudase yemwe, wompereka iye, anaima nao pamodzi.

6. Ndipo m'mene anati kwa iwo, Ndine, anabwerera m'mbuyo, nagwa pansi.

7. Pamenepo anawafunsanso, Mufuna yani? koma iwo anati, Yesu Mnazarayo.

8. Yesu anayankha, Ndati, Ndine; cifukwa cace ngati mufuna Ine, lekani awa amuke;

Werengani mutu wathunthu Yohane 18