Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 17:16-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Siali adziko lapansi monga Ine sindiri wa dziko lapansi.

17. Patulani iwo m'coonadi; mau anu ndi coonadi.

18. Monga momwe munandituma Ine ku dziko lapansi, Inenso ndinatuma iwo ku dziko lapansi,

19. Ndipo cifukwa ca iwo Ine ndidzipatula ndekha kuti iwonso akhale opatulidwa m'coonadi.

20. Koma sindipempherera iwo okha, komanso iwo akukhulupirira Ine cifukwa ca mau ao;

21. kuti onse akakhale amodzi, monga Inu Atate mwa Ine, ndi Ine mwa Inu, kuti iwonso akakhale mwa Ife: kuti dziko lapansi likakhulupire kuti Inu munandituma Ine.

22. Ndipo ulemerero umene mwandipatsa Ine ndapatsa Iwo; kuti akhale amodzi, monga Ife tiri mmodzi;

23. Ine mwa iwo, ndi Inu mwa Ine, kuti akhale angwiro mwa mmodzi; kutr dziko lapansi lizindikire kuti Inu munandituma Ine, nimunawakonda iwo, monga momwe munakonda Ine,

24. 1 Atate, amene mwandipatsa Ine, ndifuna kuti, kumene ndiri Ine, iwonso akhale pamodzi ndi Ine; kuti ayang'anire ulemerero wanga, umene mwandipatsa Ine; 2 pakuti munandikonda Inelisanakhazildke dziko lapansi.

Werengani mutu wathunthu Yohane 17