25. Izi ndalankhula nanu, pakukhala ndi inu.
26. Koma 2 Nkhosweyo, Mzimu Woyera, amene Atate adzamtuma m'dzina langa, 3 Iyeyo adzaphunzitsa Inu zonse, nadzakumbutsa inu zinthu zonse zimene ndinanena kwa inu.
27. 4 Mtendere ndikusiyirani inu, mtendere wanga ndikupatsani; Ine sindikupatsani inu monga dziko lapansi lipatsa. 5 Mtima wanu usabvutike, kapena usacite mantha.
28. Mwamva kuti Ine ndinanena kwa inu, 6 Ndimuka, ndipo ndidza kwa inu. Mukadandikonda Ine, mukadakondwera kuti ndipita kwa Atate; 7 pakuti Atate ali wamkuru ndi Ine.
29. Ndipo tsopano 8 ndakuuzani cisanacitike, kuti pamene citacitika mukakhulupire.
30. Sindidzalankhulanso zambiri ndi inu, pakuti 9 mkuru wa dziko lapansi adza; ndipo alibe kanthu mwa Ine;
31. koma kuti dziko lapansi lizindikire kuti ndikonda Atate, ndikuti 10 ndicita monga momwe Atate wandilamulira. Nyamukani, tizimuka kucokera kuno.