Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 14:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mtima wanu usabvutike; mukhulupirira Mulungu, khulupirirani Inenso.

2. M'nyumba ya Atate wanga alimo malo okhalamo ambiri. Ngati sikudali kutero, ndikadakuuzani inu; pakuti ndipita kukukonzerani inu malo.

3. Ndipo ngati ndipita kukakonzera inu malo, ndidzabweranso, ndipo ndidzalandira inu kwa Ine ndekha; kuti kumene kuli Ineko, mukakhale inunso.

4. Ndipo kumene ndinkako Ine, mudziwa njira yace.

5. Tomasi ananena ndi Iye, Ambuye, sitidziwa kumene munkako; tidziwa njira bwanji?

6. Yesu ananena naye, ine ndinenjira, ndi coonadi, ndi moyo. Palibe munthu adza kwa Atate, koma mwa Ine.

7. Mukadazindikira ine mukadadziwa Atate wanganso; kuyambira tsopano mumzindikira iye, ndipo mwamuona iye.

8. Filipo ananena ndi iye, Ambuye, tionetsereni ife Atate, ndipo citikwanira.

Werengani mutu wathunthu Yohane 14