Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 14:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mtima wanu usabvutike; mukhulupirira Mulungu, khulupirirani Inenso.

2. M'nyumba ya Atate wanga alimo malo okhalamo ambiri. Ngati sikudali kutero, ndikadakuuzani inu; pakuti ndipita kukukonzerani inu malo.

3. Ndipo ngati ndipita kukakonzera inu malo, ndidzabweranso, ndipo ndidzalandira inu kwa Ine ndekha; kuti kumene kuli Ineko, mukakhale inunso.

4. Ndipo kumene ndinkako Ine, mudziwa njira yace.

Werengani mutu wathunthu Yohane 14