Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 13:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Anadza pomwepo kwa Simoni Petro. Iyeyu ananena ndi iye, Ambuye, kodi Inu mundisambitsa ine mapazi?

7. Yesu anayankha nati kwa iye, Cimene ndicita Ine, sucidziwa tsopano; koma udzadziwa m'tsogolo mwace.

8. Petro ananena ndi iye, Simudzasambitsa mapazi anga ku nthawi yonse. Yesu anamyankha iye, Ngati sindikusambitsa iwe ulibe colandira pamodzi ndi Ine.

9. Simoni Petro ananena ndi iye, Ambuye, si mapazi anga okha, komanse manja ndi mutu.

10. Yesu ananena naye, Amene anatha kusamba alibe kusowa koma kusamba mapazi, koma ayera monse: ndipo inu ndinu oyera, koma si nonse ai.

11. Pakuti anadziwa amene adzampereka iye; cifukwa ca ici anati, Simuli oyera nonse.

Werengani mutu wathunthu Yohane 13