Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 13:35-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. 1 Mwa ici adzazindikira onse kuti muli akuphunzira anga, ngati muli naco cikondano wina ndi mnzace.

36. Simoni Petro anena ndi iye, Ambuye, mumuka kuti? Yesu anayankha, Kumene ndimukako sungathe kunditsata Ine tsopano; koma, 2 udzanditsata bwino lomwe.

37. Petro ananena ndi iye, Ambuye, sindingathe kukutsatani Inu tsopano cifukwa ninji? 3 Ndidzataya moyo wanga cifukwa ca Inu.

38. Yesu anayankha, Moyo wako kodi udzautaya cifukwa ca Ine? Indetu, indetu, ndinena kwa iwe, Asanalire tambala udzandikana Ine katatu.

Werengani mutu wathunthu Yohane 13