Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 12:6-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Koma ananena ici si cifukwa analikusamalira osauka, koma cifukwa anali mbala, ndipo pokhala nalo thumba, amabazoikidwamo.

7. Pamenepo Yesu anati, Mleke iye, pakuti anacisungira ici tsiku la kuikidwa kwanga.

8. Pakuti osauka muli nao pamodzi ndi inu nthawi zonse; koma simuli ndi Ine nthawi zonse.

9. Pamenepo khamu lalikuru la Ayuda Iinadziwa kuti ali pomwepo; ndipo anadza, si cifukwa: ca Yesu yekha, koma kuti adzaone Lazaro, amene adamuukitsa kwa akufa.

10. Koma ansembe akulu anapangana kuti akaphe Lazaronso;

11. pakuti ambiri a Ayuda anacoka cifukwa ca iye, nakhulupirira Yesu.

12. M'mawa mwace khamu lalikuru la anthu amene adadza kuphwando, pakumva kuti Yesu alinkudza ku Yerusalemu,

13. anatenga makwata a kanjedza, naturuka kukakomana ndi iye, napfuula, Hosana; wolemekezeka iye wakudza m'dzina la Ambuye, ndiye Mfumu ya Israyeli.

14. Koma Yesu, m'mene adapeza kaburu anakhala pamenepo; monga mulembedwa:

15. Usaope, mwana wamkazi wa Ziyoni; taona Mfumu yako idza wokhala pa mwana wa buru.

16. Izisanazidziwa aku phunzira ace poyamba; koma pamene Yesu analemekezedwa, pamenepo anakumbukila kuti izi zinalembedwa za iye, ndi kuti adamcitira iye izi.

17. Pamenepo khamulo limene linali pamodzi ndi iye, m'mene anaitana Lazaro kuturuka kumanda, namuukitsa kwa akufa, anacita umboni.

Werengani mutu wathunthu Yohane 12