Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 12:29-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Cifukwa cace khamu la anthu akuimirirako, ndi kuwamva ananena kuti kwagunda. Ena ananena, Mngelo walankhula ndi iye.

30. Yesu anayankha nati, Mau awa sanafika cifukwa ca Ine, koma ca inu.

31. Tsopano pali kuweruza kwa dziko ili lapansi; mkulu wa dziko ili lapansi adzatayidwa kunja tsopano,

32. Ndipo Ine, m'mene ndikakwezedwa kudziko, ndidzakoka anthu onse kwa Ine ndekha.

Werengani mutu wathunthu Yohane 12