Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 11:54-57 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

54. Cifukwa cace Yesu sanayandeyendanso poonekera mwa Ayuda, koma anacokapo kunka ku dziko loyandikira cipululu, kumudzi dzina lace Efraimu; nakhala komweko pamodzi ndi akuphunzira ace.

55. Koma Paskha wa Ayuda anali pafupi; ndipo ambiri anakwera kunka ku Yerusalemu kucoka ku miraga, usanafike Paskha, kukadziyeretsa iwo okha.

56. Pamenepo analikumfuna Yesu, nanena wina ndi mnzace poimirira iwo m'Kacisi, Muyesa bwanji inu, sadzadza kuphwando kodi?

57. Koma ansembe akulu ndi Afarisi adalamulira, kuti, munthu wina akadziwa pokhala iye, aulule, kuti akamgwire iye.

Werengani mutu wathunthu Yohane 11