Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 11:4-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Koma Yesu pamene anamva, anati, Kudwala kumene sikuli kwa imfa, koma cifukwa ca ulemerero wa Mulungu, kuti Mwana wa Mulungu alemekezedwe nako.

5. Koma Yesu anakonda Marita, ndi mbale wace, ndi Lazaro.

6. Cifukwa cace pamene anamva kuti anadwala, anakhala pamenepo pa malo pomwepo masiku awiri.

7. Ndipo pambuyo pace ananena kwa akuphunzira ace, Tiyeni tipitenso ku Yudeya.

8. Akuphunzira ananena ndi iye, Ambuye, Ayuda analikufuna kukuponyani miyala tsopano apa; ndipo munkanso komweko kodi?

9. Yesu anayankha, Kodi sikuli maora khumi ndi awiri usana? Ngati munthu ayenda usana sakhumudwa, cifukwa apenya kuunika kwa dziko lino lapansi,

10. Koma ngati munthu ayenda usiku, akhumudwa, cifukwa mulibe kuunika mwa iye.

11. Izi anati, ndipo zitatha izi ananena nao, Lazaro bwenzi lathu ali m'tulo; koma ndimuka kukamuukitsa iye tulo tace.

12. Cifukwa cace akuphunzira ace anati kwa iye, Ambuye, ngati ali m'tulo adzacira.

13. Koma Yesu adanena za imfa yace; koma iwowa anayesa kuti ananena za mpumulo wa tulo.

Werengani mutu wathunthu Yohane 11