Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 11:26-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. ndipo yense wakukhala ndi moyo, nakhulupirira Ine, sadzamwalira nthawi yonse. Kodi ukhulupirira ici?

27. Ananena ndi iye, Inde Ambuye; ndakhulupirira ine kuti Inu ndinu Kristu, Mwana wa Mulungu, wakudza m'dziko lapansi.

28. Ndipo m'mene anati ici anacoka naitana Mariya mbale wace m'tseri, ndi kuti, Wafika Mphunzitsi, akuitana iwe.

29. Koma iyeyo, pakumva, ananyamuka msanga, nadza kwa iye.

30. (Koma Yesu sanafike kumudzi, koma anali pamalo pomwe Marita adakomana ndi Iye)

Werengani mutu wathunthu Yohane 11