Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 11:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Pamenepo Yesu anati kwa iwo momveka, Lazaro wamwalira.

15. Ndipo ndikondwera cifukwa ca inu kuti kunalibe Ine komweko, cakuti mukakhulupire; koma tiyeni, tipite kwa iye.

16. Pamenepo Tomasi, wochedwa Didimo, anati kwa akuphunzira anzace, Tipite ifenso kuti tikafere naye pamodzi.

17. Ndipo pamene Yesu anadza, anapeza kuti pamenepo atakhala m'manda masiku anai.

18. Koma Betaniya anali pafupi pa Yerusalemu, nthawi yace yonga ya mastadiya khumi ndi asanu;

19. koma ambiri a mwa Ayuda adadza kwa Marita ndi Mariya, kudzawatonthoza mtima pa mlongo wao.

20. Pamenepo Marita, pakumva kuti Yesu alinkudza, anamuka kukakomana ndi iye; koma Mariya anakhalabe m'nyumba.

Werengani mutu wathunthu Yohane 11