Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 11:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Koma Yesu adanena za imfa yace; koma iwowa anayesa kuti ananena za mpumulo wa tulo.

14. Pamenepo Yesu anati kwa iwo momveka, Lazaro wamwalira.

15. Ndipo ndikondwera cifukwa ca inu kuti kunalibe Ine komweko, cakuti mukakhulupire; koma tiyeni, tipite kwa iye.

16. Pamenepo Tomasi, wochedwa Didimo, anati kwa akuphunzira anzace, Tipite ifenso kuti tikafere naye pamodzi.

17. Ndipo pamene Yesu anadza, anapeza kuti pamenepo atakhala m'manda masiku anai.

18. Koma Betaniya anali pafupi pa Yerusalemu, nthawi yace yonga ya mastadiya khumi ndi asanu;

Werengani mutu wathunthu Yohane 11