Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 11:11-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Izi anati, ndipo zitatha izi ananena nao, Lazaro bwenzi lathu ali m'tulo; koma ndimuka kukamuukitsa iye tulo tace.

12. Cifukwa cace akuphunzira ace anati kwa iye, Ambuye, ngati ali m'tulo adzacira.

13. Koma Yesu adanena za imfa yace; koma iwowa anayesa kuti ananena za mpumulo wa tulo.

14. Pamenepo Yesu anati kwa iwo momveka, Lazaro wamwalira.

15. Ndipo ndikondwera cifukwa ca inu kuti kunalibe Ine komweko, cakuti mukakhulupire; koma tiyeni, tipite kwa iye.

Werengani mutu wathunthu Yohane 11