Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 10:38-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

38. Koma ngati ndicita, mungakhale simukhulupirira Ine, khulupirirani nchitozo; kuti mukadziwe ndi kuzindikira kuti Atate ali mwa Ine, ndi ine mwa Atate.

39. Anafunanso kumgwira iye; ndipo anapulumuka m'dzanja lao.

40. Ndipo anacoka kunkanso tsidya lija la Yordano, kumalo kumene kunali Yohane analikubatiza poyamba paja; ndipo anakhala komweko.

41. Ndipo ambiri anadza kwa iye; nanena kuti, Sanacita cizindikilo Yohane; koma zinthu ziri zonse Yohane ananena za iye zinali zoona.

42. Ndipo ambiri anakhulupirira iye komweko.

Werengani mutu wathunthu Yohane 10