Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 10:30-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Ine ndi Atate ndife amodzi.

31. Ayuda anatolanso miyala kuti amponye iye.

32. Yesu anayankha iwo, ndakuonetsani inu nchito zabwino zambiri za kwa Atate; cifukwa ca nchito yiti ya izo mundiponya miyala?

33. Ayuda anamyankha iye, Cifukwa ca nchito yabwino sitikuponyani miyala, koma cifukwa ca mwano; ndi kuti Inu, muli munthu, mudziyesera nokha Mulungu,

34. Yesu anayankha iwo, Kodi sikulembedwa m'cilamulo canu, Ndinati Ine, Muli milungu?

35. Ngati anawacha milungu iwo amene mau a Mulungu anawadzera (ndipo colemba sicingathe kutyoka),

36. kodi inu munena za iye, amene Atate anampatula namtuma ku dziko lapansi, Ucita mwano; cifukwa ndinati, Ndiri Mwana wa Mulungu?

37. Ngati sindicita nchito za Atate wanga, musakhulupirira Ine.

38. Koma ngati ndicita, mungakhale simukhulupirira Ine, khulupirirani nchitozo; kuti mukadziwe ndi kuzindikira kuti Atate ali mwa Ine, ndi ine mwa Atate.

39. Anafunanso kumgwira iye; ndipo anapulumuka m'dzanja lao.

40. Ndipo anacoka kunkanso tsidya lija la Yordano, kumalo kumene kunali Yohane analikubatiza poyamba paja; ndipo anakhala komweko.

41. Ndipo ambiri anadza kwa iye; nanena kuti, Sanacita cizindikilo Yohane; koma zinthu ziri zonse Yohane ananena za iye zinali zoona.

42. Ndipo ambiri anakhulupirira iye komweko.

Werengani mutu wathunthu Yohane 10