Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 10:19-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Panakhalanso kutsutsana pakati pa Ayuda cifukwa ca mau awa.

20. Koma ambiri mwa iwo ananena, Ali ndi ciwanda, nacita misala; mukumva iye bwanji?

21. Ena ananena, Mau awa sali a munthu wogwidwa ciwanda. Kodi ciwanda cikhoza kumtsegulira maso wosaona?

22. Koma kunali phwando la kukonzersanso m'Yerusalemu; nyengoyo ndi yacisanu.

23. Ndipo Yesu analikuyendayenda m'Kacisi m'khumbi la Solomo,

24. Pamenepo Ayuda anamzungulira iye, nanena ndi iye, Kufikira liti musfnkhitsa-slnkhitsa moyo wathu? ngati Inu ndinu Kristu, tiuzeni momveka.

25. Yesu anayankha iwo, Ndakuuzani, ndipo simukhulupirira, Nchitozi ndizicita Ine m'dzina la Atate wanga, zimenezi zindicitira umboni.

26. Koma inu simukhulupira, cifukwa simuli a mwa nkhosa zanga.

27. Nkhosa zanga zimva mau anga, ndipo Ine ndizizindikira, ndipo zinditsata Ine.

Werengani mutu wathunthu Yohane 10