Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 1:40-44 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

40. Andreya mbale wace wa Simoni Petro anali mmodzi wa awiriwo, anamva Yohane, namtsata iye.

41. Anayamba iye kupeza mbale wace yekha Simoni, nanena naye, Tapeza ife Mesiya (ndiko kusandulika Kristu).

42. Anadza naye kwa Yesu. M'mene anamyang'ana iye, anati, Uli Simoni mwana wa Yohane; 11 udzachedwa Kefa (ndiko kusandulika Petro).

43. M'mawa mwace anafuna kuturuka kunka ku Galileya, napeza Filipo, Ndipo Yesu ananena naye, Tsata Ine.

44. Koma Filipo anali wa ku Betsaida, mudzi wa Andreya ndi Petro.

Werengani mutu wathunthu Yohane 1