Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 1:4-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Mwa iye munali moyo; ndi moyowu unali kuunika kwa anthu.

5. Ndipo kuunikaku kunawala mumdima; ndi mdimawu sunakuzindikira.

6. Kunali munthu, wotumidwa ndi Mulungu, dzina lace ndiye Yohane.

7. Iyeyu anadza mwa umboni kudzacita umboni za kuunikaku, kuti onse akakhulupirire mwa iye,

8. iye sindiye kuunikaku, koma anatumidwa kukacita umboni wa kuunikaku.

9. Uku ndiko kuunika kweni kweni, kumene kuunikira anthu onse akulowa m'dziko lapansi.

Werengani mutu wathunthu Yohane 1