Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 1:2-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Awa anali paciyambi kwa Mulungu,

3. Zonse: zinalengedwa ndi iye; ndipo kopanda iye sikunalengedwa kanthu kali konse kolengedwa,

4. Mwa iye munali moyo; ndi moyowu unali kuunika kwa anthu.

5. Ndipo kuunikaku kunawala mumdima; ndi mdimawu sunakuzindikira.

6. Kunali munthu, wotumidwa ndi Mulungu, dzina lace ndiye Yohane.

Werengani mutu wathunthu Yohane 1