Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 1:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Anali m'dziko lapansi, ndi dziko linalengedwa ndi iye, koma dziko silinamzindikira iye.

11. Anadza kwa zace za iye yekha, ndipo ace a mwini yekha sanamlandira iye.

12. Koma onse amene anamlandira iye, kwa iwo anapatsa mphamvu yakukhala ana a Mulungu, kwa iwotu, akukhulupirira dzina lace;

13. amene sanabadwa ndi mwazi, kapena ndi cifuniro ca thupi, kapena ndi cifuniro ca munthu, koma ca Mulungu.

14. Ndipo Mau anasandulika thupi, nakhazikika pakati pa ife, ndipo tinaona ulemerero wace, ulemerero wonga wa wobadwa yekha wa Atate, wodzala ndi cisomo ndi coonadi.

Werengani mutu wathunthu Yohane 1