Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 1:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. PACIYAMBI panali Mau, ndipo Mau anali kwa Mulungu, ndipo Mau ndiye Mulungu.

2. Awa anali paciyambi kwa Mulungu,

3. Zonse: zinalengedwa ndi iye; ndipo kopanda iye sikunalengedwa kanthu kali konse kolengedwa,

4. Mwa iye munali moyo; ndi moyowu unali kuunika kwa anthu.

5. Ndipo kuunikaku kunawala mumdima; ndi mdimawu sunakuzindikira.

6. Kunali munthu, wotumidwa ndi Mulungu, dzina lace ndiye Yohane.

7. Iyeyu anadza mwa umboni kudzacita umboni za kuunikaku, kuti onse akakhulupirire mwa iye,

Werengani mutu wathunthu Yohane 1