Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 1:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. PACIYAMBI panali Mau, ndipo Mau anali kwa Mulungu, ndipo Mau ndiye Mulungu.

2. Awa anali paciyambi kwa Mulungu,

3. Zonse: zinalengedwa ndi iye; ndipo kopanda iye sikunalengedwa kanthu kali konse kolengedwa,

4. Mwa iye munali moyo; ndi moyowu unali kuunika kwa anthu.

5. Ndipo kuunikaku kunawala mumdima; ndi mdimawu sunakuzindikira.

6. Kunali munthu, wotumidwa ndi Mulungu, dzina lace ndiye Yohane.

7. Iyeyu anadza mwa umboni kudzacita umboni za kuunikaku, kuti onse akakhulupirire mwa iye,

8. iye sindiye kuunikaku, koma anatumidwa kukacita umboni wa kuunikaku.

9. Uku ndiko kuunika kweni kweni, kumene kuunikira anthu onse akulowa m'dziko lapansi.

10. Anali m'dziko lapansi, ndi dziko linalengedwa ndi iye, koma dziko silinamzindikira iye.

11. Anadza kwa zace za iye yekha, ndipo ace a mwini yekha sanamlandira iye.

Werengani mutu wathunthu Yohane 1