Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yakobo 5:2-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Cuma canu caola ndi zobvala zanu zajiwa ndi njenjete.

3. Golidi wanu ndi siliva wanu zacita dzimbiri, ndipo dzimbiri lace lidzacita mboni zoneneza Inu ndipo zidzadya nyama yanu ngat: moto. Mwadzikundikira cuma masiku otsiriza.

4. Taonani, mphotho ya anchitowo anasenga m'minda yanu, yosungidwa ndi inu powanyenga, ipfuula; ndipo mapfuulc a osengawo adalowa m'makutu a Ambuye wa makamu.

5. Mwadyerera padziko, ndipo mwacita zokukondweretsani; mwadyetsa mitima yanu m'tsiku lakupha.

6. Munamtsutsa, munapha wolungamayo, iye sakanizainu.

7. Potero, lezani mtima, abale, kufikira kudza kwace kwa Ambuye. Taonani, wolima munda alindira cipatso cofunikatu ca dziko, ndi kuleza mtima naco kufikira cikalandira mvula ya myundo ndi masika,

8. Lezani mtima inunso, limbitsani mitima yanu; pakuti kudza kwace kwa Ambuye kuyandikira.

9. Musaipidwe wina ndi mnzace, abale, kuti mungaweruzidwe. Taonani, woweruza aima pakhomo.

10. Tengani, abale, citsanzo ca kumva zowawa ndi kuleza mtima, aneneri ameneanalankhulam'dzina la Ambuyeo

11. Taonani tiwayesera odala opirirawo; mudamva za cipiriro ca Yobu, ndipo mwaona citsiriziro ca Ambuye, kuti Ambuye ali wodzala cikondi, ndi wacifundo.

12. Koma makamaka, abale anga, musalumbire, kungakhale kuchula mwamba kapena dziko, kapena lumbiro lina liri lonse; koma inde wanu akhale inde, ndi iai wanu akha; le iai; kuti mungagwe m'ciweruziro.

Werengani mutu wathunthu Yakobo 5