Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yakobo 4:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Zicokera kuti nkhondo, zicokera kuti zolimbana mwa inu? Kodi sizicokera ku zikhumbitso zanu zocita nkhondo m'ziwalo zanu?

2. Mulakalaka, ndipo zikusowani; mukupha, nimucita kaduka, ndipo simukhoza kupeza; mulimbana, nimucita nkhondo; mulibe kanthu, cifukwa simupempha.

3. Mupempha, ndipo simulandira, popeza mupempha koipa, kuti mukacimwaze pocita zikhumbitso zanu.

4. Akazi acigololo inu, kodi simudziwa kuti ubwenzi wa dziko lapansi uti udani ndi Mulungu? Potero, iye amene afuna kukhala bwenzi la dziko lapansi adziika mdani wa Mulungu.

5. Kodi muyesa kapena kuti malembo angonena cabe? Kodi Mzimuyo adamkhalitsa mwa ife akhumbitsa kucita nsanje?

6. Koma apatsa cisomo coposa. Potero anena malembo, Mulungu akaniza odzikuza, koma apatsa cisomo odzicepetsa.

7. Potero mverani Mulungu; koma kanizani mdierekezi, ndipo adzakuthawani inu.

Werengani mutu wathunthu Yakobo 4