Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yakobo 2:6-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Koma inu mumanyoza munthu wosauka. Kodi sakusautsani inu acuma, nakukokerani iwowa ku mabwalo a mirandu?

7. Kodi sacitira mwano iwowa dzina lokomali muitanidwa nalo?

8. Koma ngati mucita cikwanirire lamulolo lacifumu, monga mwa malembo, Uzikonda mnzako monga udzikonda wekha, mucita bwino:

9. koma ngati musamala maonekedwe, mucita ucimo, ndipo mutsutsidwa ndi cilamulo monga olakwa.

Werengani mutu wathunthu Yakobo 2