Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yakobo 2:23-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. ndipo anakwaniridwa malembo onenawa, Ndipo Abrahamu anakhulupirira Mulungu, ndipo kudawerengedwa kwa iye cilungamo; ndipo anachedwa bwenzi la Mulungu.

24. Mupenya kuti munthu ayesedwa wolungama ndi nchito yace, osati ndi cikhulupiriro cokha.

25. Ndipo momwemonso sanayesedwa wolungama Rahabi mkazi wa damayo ndi nchito kodi, popeza adalandira amithenga, nawaturutsa adzere njira yina?

26. Pakuti monga thupi lopanda mzimu liri lakufa, koteronso cikhulupiriro copanda nchito ciri cakufa.

Werengani mutu wathunthu Yakobo 2