Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yakobo 2:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Abrabamu kholo lathu, sanayesedwa wolungama ndi nchito kodi, paja adapereka mwana wace Isake nsembe pa guwa la nsembe?

22. Upenya kuti cikhulupiriro cidacita pamodzi ndi nchito zace, ndipo moturuka mwa nchito cikhulupiriro cidayesedwa cangwiro;

23. ndipo anakwaniridwa malembo onenawa, Ndipo Abrahamu anakhulupirira Mulungu, ndipo kudawerengedwa kwa iye cilungamo; ndipo anachedwa bwenzi la Mulungu.

24. Mupenya kuti munthu ayesedwa wolungama ndi nchito yace, osati ndi cikhulupiriro cokha.

Werengani mutu wathunthu Yakobo 2