6. Koma apemphe ndi cikhulupiriro, wosakayika konse; pakuti wokayikayo afanana ndi pfunde la nyanja lotengeka ndi mphepo ndi kuwinduka nayo.
7. Pakuti asayese munthu uyu kuti adzalandira kanthu kwa Ambuye;
8. munthu wa mitima iwiri akhala wosinkhasinkha pa njira zace zonse.
9. Koma mbale woluluka adzitamandire pa ukulu wace;
10. pakuti adzapita monga duwa la udzu,
11. Pakuti laturuka dzuwa ndi kutentha kwace, ndipo laumitsa udzu; ndipo lathothoka duwa lace, ndi ukoma wa maonekedwe ace waonongeka; koteronso wacuma adzafota m'mayendedwe ace.
12. Wodala munthu wakupirira poyesedwa; pakuti pamene wabvomerezeka, adzalandira korona wa moyo, amene Ambuye adalonjezera iwo akumkonda iye.
13. Munthu poyesedwa, asanena, Ndiyesedwa ndi Mulungu; pakuti Mulungu sakhoza kuyesedwa ndi zoipa, ndipo iye mwini sayesa munthu:
14. koma munthu ali yense ayesedwa pamene cilakolako cace ca iye mwini cimkokera, nicimnyenga.
15. Pamenepo cilakolakoco citaima, cibala ucimo; ndipo ucimo, utakula msinkhu, ubala imfa.