Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yakobo 1:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. YAKOBO, kapolo wa Mulungu ndi wa Ambuye Yesu Kristu, kwa mafuko khumi ndi awiri a m'cibalaliko: ndikulankhulani.

2. Muciyese cimwemwe cokha, abale anga, m'mene mukugwa m'mayesero a mitundu mitundu;

3. pozindikira kuti ciyesedwe ca cikhulupiriro canu cicita cipiriro.

4. Koma cipiriro cikhale nayo nchito yace yangwiro, kuti mukakhale angwiro ndi opanda cirema, osasowa kanthu konse.

Werengani mutu wathunthu Yakobo 1