Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Tito 3:9-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. koma pewa mafunso opusa, ndi mawerengedwe a mibadwo, ndi ndeu, ndi makani a pamalamulo; pakuti sizipindulitsa, ndipo ziri zacabe.

10. Munthu wopatukira cikhulupiriro, utamcenjeza kamodzi ndi kawiri, umkanize,

11. podziwa kuti worereyo wasandulika konse, nacimwa, nakhala wodzitsutsa Yekha.

12. Pamene ndikatuma Artema kwa iwe, kapena Tukiko, cita cangu kudza kwa ine ku Nikopoli: pakuti ndatsimikiza mtima kugonerako nyengo yacisanu.

Werengani mutu wathunthu Tito 3