Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Tito 2:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma iwe, lankhula zimene ziyenera ciphunzitso colamitsa:

2. okalamba akhale odzisunga, olemekezeka, odziletsa, olama m'cikhulupiriro, m'cikondi, m'cipiriro.

3. Momwemonso akazi okalamba akhale nao makhalidwe oyenera anthu oyera, osadierekeza, osakodwa naco cikondi ca pavinyo, akuphunzitsa zokoma;

4. kuti akalangize akazi ang one akonde amuna ao, akonde ana ao,

5. akhale odziletsa, odekha, ocita m'nyumba mwao, okoma, akumvera amuna a iwo okha, kuti mau a Mulungu angacitidwe mwano.

6. Momwemonso anyamata uwadandaulire akhale odziletsa;

Werengani mutu wathunthu Tito 2