Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Tito 2:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma iwe, lankhula zimene ziyenera ciphunzitso colamitsa:

2. okalamba akhale odzisunga, olemekezeka, odziletsa, olama m'cikhulupiriro, m'cikondi, m'cipiriro.

3. Momwemonso akazi okalamba akhale nao makhalidwe oyenera anthu oyera, osadierekeza, osakodwa naco cikondi ca pavinyo, akuphunzitsa zokoma;

4. kuti akalangize akazi ang one akonde amuna ao, akonde ana ao,

5. akhale odziletsa, odekha, ocita m'nyumba mwao, okoma, akumvera amuna a iwo okha, kuti mau a Mulungu angacitidwe mwano.

6. Momwemonso anyamata uwadandaulire akhale odziletsa;

7. m'zonse udzionetsere wekha citsanzo ca nchito zabwino; m'ciphunzitse cako uonetsere cosabvunda, ulemekezeko,

8. mau olama osatsutsika; kuti iye wakutsutsana acite manyazi, posakhala nako kanthu koipa kakutinenera ife.

9. Akapolo amvere ambuye ao a iwo okha, nawakondweretse m'zonse; osakana mau ao;

10. osatapa pa zao, komatu aonetsere cikhulupiriko conse cabwino; kuti akakometsere ciphunzitso ca Mpulumutsi wathu Mulungu m'zinthu zonse.

Werengani mutu wathunthu Tito 2