Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Tito 1:4-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. kwa Tito, mwana wanga weni weni monga mwa cikhulupiriro ca ife tonse: Cisomo ndi mtendere za kwa Mulungu Atate ndi Kristu Yesu Mpulumutsi wathu.

5. Cifukwa ca ici ndinakusiya iwe m'Krete, kuti ukalongosole zosowa, nukaike akuru m'midzi yonse, monga ndinakulamulira;

6. ngati wina ali wopanda cirema, mwamuna wa mkazi mmodzi, wokhala nao ana okhulupirira, wosasakaza zace, kapena wosakana kumvera mau.

7. Pakuti woyang'anira ayenera kukhala wopanda cirema, ngati mdindo wa Mulungu; wosati waliuma, wosapsa mtima msanga, wosati waciwawa, wopanda ndeu, wosati wa cisiriro conyansa;

8. komatu wokonda kucereza alendo, wokonda zokoma, wodziweruza, wolungama, woyera mtima, wodziletsa;

9. wogwira mau okhulupirika monga mwa ciphunzitso, kuti akakhoze kucenjeza m'ciphunzitso colamitsa, ndi kutsutsa otsutsana naye.

10. Pakuti alipo ambiri osamvera mau, olankhula zopanda pace, ndi onyenga, makamaka iwo a kumdulidwe,

11. amene ayenera kutsekedwa pakamwa; ndiwo amene apasula mabanja banja lonse, ndi kuphunzitsa zosayenera cifukwa ca cisiriro conyansa.

12. Wina wa mwa iwo, ndiye mneneri wa iwo okha, anati, Akrete ndiwo amabodza masiku onse, zirombo zoipa, aumbombo, aulesi.

13. Umboni uwu uli woona. Mwa ici uwadzudzule mokaripa, kuti akakhale olama m'cikhulupiriro,

Werengani mutu wathunthu Tito 1