Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mateyu 28:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo pamene anamuona Iye, anamlambira; koma ena anakayika.

18. Ndipo Yesu anadza nalankhula nao, nanena, Mphamvu zonse zapatsidwa kwa Ine Kumwamba ndi pa dziko lapansi.

19. Cifukwa cace mukani, phunzitsani anthu a mitundu yonse, ndi kuwabatiza iwo m'dzina la Atate, ndi la Mwana, ndi la Mzimu Woyera:

20. ndi kuwaphunzitsa, asunge zinthu zonse zimene ndinakulamulirani inu; ndipo onani, Ine ndiri pamodzi ndi inu masiku onse, kufikira cimariziro ca nthawi ya pansi pano.

Werengani mutu wathunthu Mateyu 28