Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mateyu 28:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo popita dzuwa la Sabata, mbanda kuca, tsiku lakuyamba la sabata, anadza Mariya wa Magadala, ndi Mariya winayo, kudzaona manda.

2. Ndipo onani, panali cibvomezi cacikuru; pakuti mngelo wa Ambuye anatsika Kumwamba, nafika kukunkhuniza mwalawo, nakhala pamwamba pace.

3. Kuonekera kwace kunali ngati mphezi, ndi cobvala cace coyeretsa ngati matalala;

4. ndipo ndi kuopsa kwace alondawo ananthunthumira, nakhala ngati anthu akufa.

5. Koma mngelo anayankha, nati kwa akaziwo, Musaope inu; pakuti ndidziwa inu mulikufuna Yesu, amene anapacikidwa.

6. Iye mulibe muno iai; pakuti anauka, monga ananena. Idzani muno mudzaone malo m'mene anagonamo Ambuye.

7. Ndipo pitani msanga, muuze ophunzira ace, kuti, Wauka kwa akufa; ndipo onani, akutsogolerani ku Galileya; mudzamuona Iye komweko; onani, ndakuuzani inu.

8. Ndipo iwo anacoka msanga kumanda, ndi mantha ndi kukondwera kwakukuru, nathamanga kukauza ophunzira ace.

9. Ndipo onani, Yesu anakomana nao, nanena, Tikuoneni. Ndipo iwo anadza, namgwira Iye mapazi ace, namgwadira.

Werengani mutu wathunthu Mateyu 28