Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 9:33-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

33. Ndipo iwo anadza ku Kapernao; ndipo pamene anakhala m'nyumba, Iye anawafunsa, Munalikutsutsana ninji panjira?

34. Koma iwo anakhala cete; pakuti anatsutsana wina ndi mnzace panjira, kuti, wamkuru ndani?

35. Ndipo m'mene anakhala pansi anaitana khumi ndi awiriwo; nanena nao, Ngati munthu afuna kukhala woyamba, akhale wakuthungo wa onse, ndi mtumiki wa onse.

36. Ndipo anatenga kamwana, nakaika pakati pao, nakayangata, nanena nao,

37. Munthu ali yense adzalandira kamodzi ka tiana totere cifukwa ca dzina langa, alandira ine; ndipo yense amene akalandira Ine, salandira Ine, koma Iye amene anandituma Ine.

38. Yohane anati kwa Iye, Mphunzitsi, tinaona munthu alikuturutsa ziwanda m'dzina lanu; ndipo tinamletsa, cifukwa sanalikutsata ife.

Werengani mutu wathunthu Marko 9