Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 8:9-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo iwo anali ngati zikwi zinai; ndipo Iye analawirana nao.

10. Ndipo pomwepo analowa m'ngaiawa ndi akhupunzira ace, nafika ku mbali ya ku Dalmanuta.

11. Ndipo Afarisi anaturuka, nayamba kufunsana naye, ndi kufuna kwa Iye cizindikilo cocokera Kumwamba, namuyesa Iye.

12. Ndipo anausitsa moyo m'mzimu wace, nanena, Anthu a mbadwo uno afunafuna cizindikilo bwanji? indetu ndinena kwa inu, ngati cizindikilo cidzapatsidwa kwa mbadwo uno!

13. Ndipo anawasiya iwo, nalowanso m'ngalawa, nacoka kunka ku tsidya lija.

14. Ndipo ophunzira adaiwala kutenga mikate, ndipo analibe mkate m'ngalawa koma umodzi wokha.

15. Ndipo Iye anawalamula, nanena, Yang'anirani, penyani kuti mupewe cotupitsa mkate ca Afarisi, ndi cotupitsa mkate ca Herode.

16. Ndipo anatsutsana wina ndi mnzace, nanena kuti, Tiribe mikate.

17. Ndipo Yesu pamene anazindikira, ananena nao, Bwanji mutsutsana cifukwa mulibe mkate? kodi kufikira tsopano simuzindikira, nisimudziwitsa? kodi muli nayo mitima yanu youma?

Werengani mutu wathunthu Marko 8