Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 8:6-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo analamulira anthu a khamulo akhale pansi; natenga mikate isanu ndi iwiriyo, nayamika, nanyema, napatsa ophunzira ace, kuti apereke kwa iwo; ndipo anapereka kwa khamulo.

7. Ndipo anali nato tinsomba towerengeka; ndipo Iye anatidalitsa, nati atipereke itonso.

8. Ndipo anadya nakhuta; ndipo anatola makombo malicero asanu ndi awiri.

9. Ndipo iwo anali ngati zikwi zinai; ndipo Iye analawirana nao.

10. Ndipo pomwepo analowa m'ngaiawa ndi akhupunzira ace, nafika ku mbali ya ku Dalmanuta.

11. Ndipo Afarisi anaturuka, nayamba kufunsana naye, ndi kufuna kwa Iye cizindikilo cocokera Kumwamba, namuyesa Iye.

12. Ndipo anausitsa moyo m'mzimu wace, nanena, Anthu a mbadwo uno afunafuna cizindikilo bwanji? indetu ndinena kwa inu, ngati cizindikilo cidzapatsidwa kwa mbadwo uno!

13. Ndipo anawasiya iwo, nalowanso m'ngalawa, nacoka kunka ku tsidya lija.

Werengani mutu wathunthu Marko 8