Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 7:7-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Koma andilambira Ine kwacabe,Ndi kuphunzitsa maphunzitso, malangizo a anthu.

8. Musiya lamulo la Mulungu, nimusunga mwambo wa anthu.

9. Ndipo ananena nao, Bwino mukaniza lamulo la Mulungu, kuti musunge mwambo wanu,

10. Pakuti Mose anati, Lemekeza atate wako ndi amako; ndipo iye wakunenera zotpa atate wace kapena amai wace, afe ndithu;

11. koma inu munena, Munthu akati kwa atate wace, kapena amai wace, Karban, ndiko kuti Mtulo, cimene ukadathandizidwa naco ndi ine,

12. simulolanso kumcitira kanthu atate wace kapena amai wace;

13. muyesa acabe mau a Mulungu mwa mwambo wanu, umene munaupereka: ndi zinthu zotere zambiri muzicita.

14. Ndipo anadziitaniranso khamu la anthu, nanena nao, Mverani Ine nonsenu, ndipo dziwitsani:

15. kulibe kanthu kunja kwa munthu kakulowa mwa iye, kangathe kumdetsa: koma zinthu zakuturuka mwa munthu, ndizo zakumdetsa munthu.[

Werengani mutu wathunthu Marko 7