Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 7:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo Iye ananena nao, Yesaya ananenera bwino za inu onyenga, monga mwalembedwa,Anthu awa andilemekeza Ine ndi milomo yao,Koma mtima wao ukhala kutari ndi ine.

7. Koma andilambira Ine kwacabe,Ndi kuphunzitsa maphunzitso, malangizo a anthu.

8. Musiya lamulo la Mulungu, nimusunga mwambo wa anthu.

9. Ndipo ananena nao, Bwino mukaniza lamulo la Mulungu, kuti musunge mwambo wanu,

10. Pakuti Mose anati, Lemekeza atate wako ndi amako; ndipo iye wakunenera zotpa atate wace kapena amai wace, afe ndithu;

11. koma inu munena, Munthu akati kwa atate wace, kapena amai wace, Karban, ndiko kuti Mtulo, cimene ukadathandizidwa naco ndi ine,

Werengani mutu wathunthu Marko 7