Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 7:34-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. nagadamira kumwamba, nausa moyo, nanena naye, Elata, ndiko, Tatseguka.

35. Ndipo makutu ace anatseguka, ndi comangira lilime lace cinamasulidwa, ndipo analankhula cilunjikire.

36. Ndipo anawalamulira kuti asauze munthu, ali yense; koma monga momwe Iye anawalamulitsa momwenso makamaka analalikira kopambana.

37. Ndipo anadabwa kwakukurukuru, nanena, Wacita Iye zonse bwino; angakhale ogontha awamvetsa, ndi osalankhula awalankhulitsa.

Werengani mutu wathunthu Marko 7