31. Ndipo anaturukanso m'maiko a ku Turo, nadzera pakati pa Sidoni, cufikira ku nyanja ya Galileya, ndi cupyola pakati pa maiko a ku Dekapolio
32. Ndipo anadza naye kwa Iye munthu wogontha, ndi wacibwibwi; ndipo anampempha Iye kuti aike dzanja pa iye.
33. Ndipo anampatula pa khamu la anthu pa yekha, nalonga zala zace m'makutu mwace, nalabvula malobvu, nakhudza lilime lace:
34. nagadamira kumwamba, nausa moyo, nanena naye, Elata, ndiko, Tatseguka.