Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 7:31-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Ndipo anaturukanso m'maiko a ku Turo, nadzera pakati pa Sidoni, cufikira ku nyanja ya Galileya, ndi cupyola pakati pa maiko a ku Dekapolio

32. Ndipo anadza naye kwa Iye munthu wogontha, ndi wacibwibwi; ndipo anampempha Iye kuti aike dzanja pa iye.

33. Ndipo anampatula pa khamu la anthu pa yekha, nalonga zala zace m'makutu mwace, nalabvula malobvu, nakhudza lilime lace:

34. nagadamira kumwamba, nausa moyo, nanena naye, Elata, ndiko, Tatseguka.

Werengani mutu wathunthu Marko 7