Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 7:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo m'mene Iye adalowa m'nyumba kusiyana ndi khamulo, ophunzira ace anamfunsa Iye faruzolo.

18. Ndipo ananena nao, Mutero inunso opanda nzeru kodi? Kodi simuzindikira kuti kanthu kali konse kocokera kunja kakulowa mwa munthu, sikangathe kumdetsa iye;

19. cifukwa sikalowa mumtima mwace, koma m'mimba mwace, ndipo katurukira kuthengo? Ndipo potero anayeretsa zakudya zonse.

20. Ndipo anati, Coturuka mwa munthu ndico cidetsa munthu.

21. Pakuti m'kati mwace mwa mitima ya anthu, muturuka maganizo oipa, zaciwerewere,

22. zakuba, zakupha, zacigololo, masiriro, zoipa, cinyengo, cinyanso, diso loipa, mwano, kudzikuza, kupusa:

Werengani mutu wathunthu Marko 7